Pastor Patrick Makhumula anabadwa pa 11 October, 1979 ndipo m’banja mwawo anabadwa ana khumi,amuna asanu,akazinso asanu ndipo iwo ndi achitatu kubadwa. Pastor Makhumula amachokera ku Blantyre, ku Mdeka m’mudzi mwa a Nthache, T/A Chigaru koma pakadali pano akukhalira ku South Africa mumzinda wa Durban komwe akugwiranso ntchito.

Pastor Makhumula anayambila kuyimba ku Sunday School ndipo amakula ali muchimenecho ndipo kwa iwo mayimbidwe ndimayitanidwe.
Pastor Makhumula atulutsako nyimbo zatsopano zitatu mu mwezi wa March chaka chino monga Ndili pano, Mulinane komaso Ndidalira Inu.