Sylvia Shaba oyimba wa ku Malawi amachokera M’boma la Mzimba ndipo anabadwa pa 13 September, 1984 ndipo wakulira ku Mzimba komko dera la Manyamula m’mudzi mwa Zikhole Sakala.
Mu banja mwawo anabadwa ana 6 otsala atatu omwe anamwalira atatunso. Kwa iyeyu kuyimba ndi mayitanidwe kuchokera ali wachichepere, nthawi yomwe anali wachichepere ankakonda zoyimba monga ma choirs komanso ma fellowship.
Sylvia ali ku school atakwanitsa zaka 11 analota maloto oti ali pakati pa chimzinda chachikuru akuyambitsa nyimbo yoti ndilandireni ine mbuye komanso nyimbo ina yotchedwa Hallelujah mwakuti anachikhazikitsa pansi pa mtima wake kuti iye adzatumikira Mulungu moyo wake onse.
Sylvia wayimbapo ndi ma choirs ambiri moti mwa ena anaturutsa nawo chimbale monga Manyamula Manse Choir ndi ma Band ena mu dela la Rumphi Mpherembe ndipo pachimenechi Sylvia analimbikitsidwa kuziyimira payekha mkuturutsa ma audio ake.
Sylvia ndi mayi oti ali ndi ana awiri ndipo oyamba ali ndi zaka 19 pomwe wachiwiri ali ndi zaka 15 ndipo poonjezera apo amasamaliranso ana atatu omwe ndi a malemu sister wake kusonyeza ali ndi ana 5 ndipo Sylvia ndi single Mom ndipo akukhala ku Durban North City m’dziko la South Africa ndipo ndikumene waturutsila ma audios ake.