Home LyricsJanet Smart – Ndayimba Foni Lyrics

Janet Smart – Ndayimba Foni Lyrics

by Kuwala Gospel Music
185 views

Chorus 

Ndaimba foni kumwamba Ambuye wandiyakha zokhumba mtima wanga zosowa pamoyo wanga Ambuye wandiyakha                         

Verse 1                            

Ndinali ndani ine pamaso pa anthuwa amzanga kundiseka abale kundisala abwenzi kundithawa koma inu Ambuye munachita kuthekera pano moyo wanga ndiwodalitsika mukhale nane Ambuye

 Chorus

Ndayimba foni kumwamba Ambuye wandiyakha zokhumba mtima wanga zosowa pa moyo wanga Ambuye wandiyankha                       

Verse 2

Mukhale nane Ambuye  munyengo ya mavuto munyengo ya mtendere ngakhale mu chilichonse muyende nane Ambuye ndinu odabwitsa mumachita chinthu chilichonse pakuti moyo wanga munawulenga kale munandidziwa ine.